MANJA  A NTCHITO YA MULUNGU (#13471)

Kuwala ndi ulemelero, malonje ndi mayamiko zikhale pa Manja a Ntchito Yake amene kupyolera mwa iwo nyali yobvutika nthawi – yaitali, yawala, ndi kukhazikitsidwa kwa udindo kunazindikirika kuti nkuchokera kwa Mulungu, Wamphamvu, Wamkulu, Wapayekha ndi kupyolera mwa omwe nyanja yopatsa iyendayenda, ndi mphepo ya chifundo cha Mulungu, Ambuye wa anthu onse, yauziridwa. Ife tipempha mwa Iye – wam’mwamba Ndiye – kuti awachinjirize iwo ndi magulu Ake, kuwayang’anira ndi ufumu Wake, ndi kuwathandiza ndi mphamvu Zake zomwe zagonjetsa zinthu zonse, Ufumu ndi wa Mulungu, Wolenga za kumwamba, ndi Mfumu wa Ufumu wa Maina onse.

-Bahá'u'lláh
-----------------------

